Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:41-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova,Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.

42. Kuti ndikhale nao mau akuyankha wonditonza;Popeza ndikhulupirira mau anu.

43. Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga;Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.

44. Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.

45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

47. Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.

48. Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49. Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.

50. Citonthozo canga m'kuzunzika kwanga ndi ici;Pakuti mau anu anandipatsa moyo.

51. Odzikuza anandinyoza kwambiri:Koma sindinapatukanso naco cilamulo canu.

52. Ndinakumbukila maweruzo anu kuyambira kale, Yehova,Ndipo ndinadzitonthoza.

53. Ndinasumwa kwakukuru,Cifukwa ca oipa akusiya cilamulo canu.

54. Malemba anu anakhala nyimbo zangaM'nyumba ya ulendo wanga,

55. Usiku ndinakumbukila dzina lanu, Yehova,Ndipo ndinasamalira cilamulo canu.

56. Ici ndinali naco,Popeza ndinasunga malangizo anu.

57. Yehova ndiye gawo langa:Ndinati ndidzasunga mau anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119