Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:40-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Taonani, ndinalira malangizo anu;Mundipatse moyo mwa cilungamo canu.

41. Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova,Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.

42. Kuti ndikhale nao mau akuyankha wonditonza;Popeza ndikhulupirira mau anu.

43. Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga;Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.

44. Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.

45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

47. Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.

48. Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49. Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119