Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:36-53 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu,Si ku cisiriro ai.

37. Mucititse mlubza maso anga ndisapenye zacabe,Mundipatse moyo mu njira yanu.

38. Limbitsirani mtumiki wanu mau anu,Ndiye wodzipereka kukuopani.

39. Mundipatutsire cotonza canga ndiciopaco;Popeza maweruzo anu ndi okoma.

40. Taonani, ndinalira malangizo anu;Mundipatse moyo mwa cilungamo canu.

41. Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova,Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.

42. Kuti ndikhale nao mau akuyankha wonditonza;Popeza ndikhulupirira mau anu.

43. Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga;Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.

44. Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.

45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

47. Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.

48. Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49. Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.

50. Citonthozo canga m'kuzunzika kwanga ndi ici;Pakuti mau anu anandipatsa moyo.

51. Odzikuza anandinyoza kwambiri:Koma sindinapatukanso naco cilamulo canu.

52. Ndinakumbukila maweruzo anu kuyambira kale, Yehova,Ndipo ndinadzitonthoza.

53. Ndinasumwa kwakukuru,Cifukwa ca oipa akusiya cilamulo canu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119