Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:35-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Mundiyendetse mopita malamulo anu;Pakuti ndikondwera m'menemo.

36. Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu,Si ku cisiriro ai.

37. Mucititse mlubza maso anga ndisapenye zacabe,Mundipatse moyo mu njira yanu.

38. Limbitsirani mtumiki wanu mau anu,Ndiye wodzipereka kukuopani.

39. Mundipatutsire cotonza canga ndiciopaco;Popeza maweruzo anu ndi okoma.

40. Taonani, ndinalira malangizo anu;Mundipatse moyo mwa cilungamo canu.

41. Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova,Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.

42. Kuti ndikhale nao mau akuyankha wonditonza;Popeza ndikhulupirira mau anu.

43. Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga;Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.

44. Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.

45. Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46. Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119