Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.

28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.

29. Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.

30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,

31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119