24. Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.
25. Moyo wanga umamatika ndi pfumbi;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.
26. Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha:Mundiphunzitse malemba anu.
27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.
28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.
29. Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.
30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,
31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.
32. Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.
33. Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu;Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.
34. Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu;Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.