170. Kupemba kwanga kudze pamaso panu;Mundilanditse monga mwa mau anu.
171. Milomo yanga iturutse cilemekezo;Popeza mundiphunzitsa malemba anu.
172. Lilime langa liyimbire mau anu;Pakuti malamulo anu onse ndiwo olungama.
173. Dzanja lanu likhale lakundithandizaPopezandinasankha malangizo anu.
174. Ndinakhumba cipulumutso canu, Yehova;Ndipo cilamulo canu ndico condikondweretsa.
175. Mzimu wanga ukhale ndi moyo, ndipo udzakulemekezani;Ndipo maweruzo anu andithandize.
176. Ndinasocera ngati nkhosa yotayika; funani mtumiki wanu;Pakuti sindiiwala malamulo anu.