168. Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu;Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,
169. Kupfuula kwanga kuyandikire pamaso pano, Yehova;Mundizindikiritse monga mwa mau anu.
170. Kupemba kwanga kudze pamaso panu;Mundilanditse monga mwa mau anu.
171. Milomo yanga iturutse cilemekezo;Popeza mundiphunzitsa malemba anu.