Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:155-171 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

155. Cipulumutso citalikira oipa;Popeza safuna malemba anu.

156. Zacifundo zanu ndi zazikuru, Yehova;Mundipatse moyo monga mwa maweruzo anu.

157. Ondilondola ndi ondisautsa ndiwoambiri;Koma sindinapatukana nazo mboni zanu.

158. Ndinapenya ocita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao;Popeza sasamalira mau anu.

159. Penyani kuti ndikonda malangizo anu;Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.

160. Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi;Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

161. Nduna zinandilondola kopanda cifukwa;Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.

162. Ndikondwera nao mau anu,Ngati munthu wakupeza zofunkha zambiri.

163. Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.

164. Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi,Cifukwa ca maweruzo anu alungama.

165. Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri;Ndipo alibe cokhumudwitsa.

166. Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.

167. Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.

168. Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu;Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,

169. Kupfuula kwanga kuyandikire pamaso pano, Yehova;Mundizindikiritse monga mwa mau anu.

170. Kupemba kwanga kudze pamaso panu;Mundilanditse monga mwa mau anu.

171. Milomo yanga iturutse cilemekezo;Popeza mundiphunzitsa malemba anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119