Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:151-159 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

151. Inu muli pafupi, Yehova;Ndipo malamulo anu onse ndiwo coonadi,

152. Kuyambira kale ndinadziwa mu mboni zanu,Kuti munazikhazika kosatha,

153. Penyani kuzunzika kwanga, nimundilanditse;Pakuti sindiiwala cilamulo canu.

154. Mundinenere mlandu wanga, nimundiombole;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

155. Cipulumutso citalikira oipa;Popeza safuna malemba anu.

156. Zacifundo zanu ndi zazikuru, Yehova;Mundipatse moyo monga mwa maweruzo anu.

157. Ondilondola ndi ondisautsa ndiwoambiri;Koma sindinapatukana nazo mboni zanu.

158. Ndinapenya ocita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao;Popeza sasamalira mau anu.

159. Penyani kuti ndikonda malangizo anu;Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119