Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:144-154 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

144. Mboni zanu ndizo zolungama kosatha;Mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.

145. Ndinaitana ndi mtima wanga wonse; mundiyankhe, Yehova;Ndidzasunga malemba anu.

146. Ndinaitanira Inu; ndipulumutseni,Ndipo ndidzasamalira mboni zanu.

147. Ndinapfuula kusanace:Ndinayembekezera mau anu.

148. Maso anga anakumika malonda a usiku,Kuti ndilingirire mau anu.

149. Imvani liu langa monga mwa cifundo canu;Mundipatse moyo monga mwa kuweruza kwanu, Yehova.

150. Otsata zaciwembu andiyandikira;Akhala kutali ndi cilamulo canu.

151. Inu muli pafupi, Yehova;Ndipo malamulo anu onse ndiwo coonadi,

152. Kuyambira kale ndinadziwa mu mboni zanu,Kuti munazikhazika kosatha,

153. Penyani kuzunzika kwanga, nimundilanditse;Pakuti sindiiwala cilamulo canu.

154. Mundinenere mlandu wanga, nimundiombole;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119