Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:14-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,

15. Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.

16. Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,

17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.

18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.

19. Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;Musandibisire malamulo anu.

20. Mtima wanga wasweka ndi kukhumbaMaweruzo anu nyengo zonse.

21. Munadzudzula odzikuza otembereredwa,Iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.

22. Mundicotsere cotonza, ndi cimpepulo;Pakuti ndinasunga mboni zanu.

23. Nduna zomwe zinakhala zondineneza;Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.

24. Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.

25. Moyo wanga umamatika ndi pfumbi;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

26. Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha:Mundiphunzitse malemba anu.

27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.

28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.

29. Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.

30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,

31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.

32. Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.

33. Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu;Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.

34. Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu;Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119