14. Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,
15. Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.
16. Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,
17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.
18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.
19. Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;Musandibisire malamulo anu.