Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:136-149 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

136. Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi,Popeza sasamalira cilamulo canu.

137. Inu ndinu wolungama, Yehova,Ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.

138. Mboni zanuzo mudazilamuliraZiri zolungama ndi zokhulupirika ndithu.

139. Cangu canga cinandithera,Popeza akundisautsa anaiwala mau anu.

140. Mau anu ngoyera ndithu;Ndi mtumiki wanu awakonda.

141. Wamng'ono ine, ndi wopepulidwa;Koma sindiiwala malemba anu.

142. Cilungamo canu ndico cilungamo cosatha;Ndi cilamulo canu ndico coonadi.

143. Kusautsika ndi kupsinjika kwandigwera;Koma malamulo anu ndiwo ondikondweretsa ine.

144. Mboni zanu ndizo zolungama kosatha;Mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.

145. Ndinaitana ndi mtima wanga wonse; mundiyankhe, Yehova;Ndidzasunga malemba anu.

146. Ndinaitanira Inu; ndipulumutseni,Ndipo ndidzasamalira mboni zanu.

147. Ndinapfuula kusanace:Ndinayembekezera mau anu.

148. Maso anga anakumika malonda a usiku,Kuti ndilingirire mau anu.

149. Imvani liu langa monga mwa cifundo canu;Mundipatse moyo monga mwa kuweruza kwanu, Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119