Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:130-143 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

130. Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.

131. Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.

132. Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo,Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.

133. Kfiazikitsanimapaziangam'mau anu;Ndipo zisandigonjetse zopanda pace ziri zonse.

134. Mundiombole ku nsautso ya munthu:Ndipo ndidzasamalira malangizo anu.

135. Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu;Ndipo mundiphunzitse malemba anu.

136. Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi,Popeza sasamalira cilamulo canu.

137. Inu ndinu wolungama, Yehova,Ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.

138. Mboni zanuzo mudazilamuliraZiri zolungama ndi zokhulupirika ndithu.

139. Cangu canga cinandithera,Popeza akundisautsa anaiwala mau anu.

140. Mau anu ngoyera ndithu;Ndi mtumiki wanu awakonda.

141. Wamng'ono ine, ndi wopepulidwa;Koma sindiiwala malemba anu.

142. Cilungamo canu ndico cilungamo cosatha;Ndi cilamulo canu ndico coonadi.

143. Kusautsika ndi kupsinjika kwandigwera;Koma malamulo anu ndiwo ondikondweretsa ine.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119