127. Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,
128. Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.
129. Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,
130. Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.
131. Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.
132. Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo,Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.