122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.
123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.
124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,
125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.
126. Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.