Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:120-132 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

120. Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu;Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.

121. Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.

122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.

123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.

124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,

125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.

126. Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.

127. Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,

128. Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.

129. Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,

130. Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.

131. Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.

132. Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo,Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119