120. Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu;Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.
121. Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.
122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.
123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.
124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,
125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.
126. Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.
127. Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,
128. Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.
129. Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,
130. Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.
131. Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.