Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:110-126 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

110. Oipa anandichera msampha;Koma sindinasokera m'malangizo anu.

111. Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha;Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

112. Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu,Kosatha, kufikira cimatiziro.

113. Ndidana nao a mitima iwiri;Koma ndikonda cilamulo canu.

114. Inu ndinu pobisalapo panga, ndi cikopa canga;Ndiyembekezera mau anu.

115. Mundicokere ocita zoipa inu;Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

116. Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.

117. Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa,Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.

118. Mupepulaonseakusokeram'malemba anu;Popeza cinyengo cao ndi bodza.

119. Mucotsa oipa onse a pa dziko lapansi ngati mphala:Cifukwa cace ndikonda mboni zanu.

120. Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu;Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.

121. Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.

122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.

123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.

124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,

125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.

126. Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119