Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:110-117 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

110. Oipa anandichera msampha;Koma sindinasokera m'malangizo anu.

111. Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha;Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

112. Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu,Kosatha, kufikira cimatiziro.

113. Ndidana nao a mitima iwiri;Koma ndikonda cilamulo canu.

114. Inu ndinu pobisalapo panga, ndi cikopa canga;Ndiyembekezera mau anu.

115. Mundicokere ocita zoipa inu;Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

116. Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.

117. Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa,Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119