108. Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga,Ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.
109. Moyo wanga ukhala m'dzanja langa cikhalire;Koma sindiiwala cilamulo canu.
110. Oipa anandichera msampha;Koma sindinasokera m'malangizo anu.
111. Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha;Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.
112. Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu,Kosatha, kufikira cimatiziro.
113. Ndidana nao a mitima iwiri;Koma ndikonda cilamulo canu.
114. Inu ndinu pobisalapo panga, ndi cikopa canga;Ndiyembekezera mau anu.
115. Mundicokere ocita zoipa inu;Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.
116. Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.
117. Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa,Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.
118. Mupepulaonseakusokeram'malemba anu;Popeza cinyengo cao ndi bodza.
119. Mucotsa oipa onse a pa dziko lapansi ngati mphala:Cifukwa cace ndikonda mboni zanu.
120. Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu;Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.
121. Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.
122. Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.
123. Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.
124. Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,
125. Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.