Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:107-113 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

107. Ndazunzika kwambiri:Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

108. Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga,Ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

109. Moyo wanga ukhala m'dzanja langa cikhalire;Koma sindiiwala cilamulo canu.

110. Oipa anandichera msampha;Koma sindinasokera m'malangizo anu.

111. Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha;Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

112. Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu,Kosatha, kufikira cimatiziro.

113. Ndidana nao a mitima iwiri;Koma ndikonda cilamulo canu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119