Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 119:1-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Odala angwiro m'mayendedwe ao,Akuyenda m'cilamulo ca Yehova.

2. Odala iwo akusunga mboni zace,Akumfuna ndi mtima wonse;

3. Inde, sacita cosalungama;Ayenda m'njira zace.

4. Inu munatilamulira.Tisamalire malangizo anu ndi cangu,

5. Ha! mwenzi zitakhazikika njira zangaKuti ndisamalire malemba anu.

6. Pamenepo sindidzacita manyazi,Pakupenyerera malamulo anu onse.

7. Ndidzakuyanrikani ndi mtima woongoka,Pakuphunzira maweruzo anu olungama.

8. Ndidzasamalira malemba anu:Musandisiye ndithu.

9. Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ace bwanji?Akawasamalira monga mwa mau anu.

10. Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse;Ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

11. Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga,Kuti ndisalakwire Inu.

12. Inu ndinu wodala Yehova;Ndiphunzitseni malemba anu.

13. Ndinafotokozera ndi milomo yangaMaweruzo onse a pakamwa panu,

14. Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,

15. Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.

16. Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,

17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.

18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 119