Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 116:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ubwere moyo wanga ku mpumulo wako;Pakuti Yehova anakucitira cokoma.

8. Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa,Maso anga kumisozi, Mapazi anga, ndingagwe.

9. Ndidzayenda pamaso pa Yehova M'dziko la amoyo.

10. Ndinakhulupirira, cifukwa cace ndinalankhula;Ndinazunzika kwambiri.

11. Pofulumizidwa mtima ndinati ine,Anthu Onse nga mabodza.

12. Ndidzabwezera Yehova cianiCifukwa ca zokoma zace zonse anandicitira?

13. Ndidzanyamula cikho ca cipulumutso,Ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova,

14. Ndidzacitazowindazanga za kwa Yehova,Tsopano, pamaso pa anthu ace onse.

15. Imfa ya okondedwa aceNja mtengo wace pamaso pa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 116