5. Yehova ngwa cifundo ndi wolungama;Ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.
6. Yehova asunga opusa;Ndidafoka ine, koma anandipulumutsa,
7. Ubwere moyo wanga ku mpumulo wako;Pakuti Yehova anakucitira cokoma.
8. Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa,Maso anga kumisozi, Mapazi anga, ndingagwe.
9. Ndidzayenda pamaso pa Yehova M'dziko la amoyo.