Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 116:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pamenepo ndinaitana dzina la Yehova;Ndikuti, Yehova ndikupemphani landitsani moyo wanga.

5. Yehova ngwa cifundo ndi wolungama;Ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.

6. Yehova asunga opusa;Ndidafoka ine, koma anandipulumutsa,

7. Ubwere moyo wanga ku mpumulo wako;Pakuti Yehova anakucitira cokoma.

8. Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa,Maso anga kumisozi, Mapazi anga, ndingagwe.

9. Ndidzayenda pamaso pa Yehova M'dziko la amoyo.

10. Ndinakhulupirira, cifukwa cace ndinalankhula;Ndinazunzika kwambiri.

11. Pofulumizidwa mtima ndinati ine,Anthu Onse nga mabodza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 116