14. Ndidzacitazowindazanga za kwa Yehova,Tsopano, pamaso pa anthu ace onse.
15. Imfa ya okondedwa aceNja mtengo wace pamaso pa Yehova.
16. Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu;Ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;Mwandimasulira zondimanga,
17. Ndidzapereka kwa Inu nsembe yaciyamiko,Ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.
18. Ndidzacita zowinda zanga za kwa Yehova,Tsopano, pamaso pa anthu ace onse;
19. M'mabwalo a nyumba ya Yehova,Pakati pa inu, Yerusalemu. Haleluya.