Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 116:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndimkonda, popeza Yehova amamva,Mau anga ndi kupemba kwanga.

2. Popeza amandicherera khutu lace,Cifukwa cace ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

3. Zingwe za imfa zinandizinga,Ndi zowawa za manda zinandigwira:Ndinapeza nsautso ndi cisoni.

4. Pamenepo ndinaitana dzina la Yehova;Ndikuti, Yehova ndikupemphani landitsani moyo wanga.

5. Yehova ngwa cifundo ndi wolungama;Ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.

6. Yehova asunga opusa;Ndidafoka ine, koma anandipulumutsa,

7. Ubwere moyo wanga ku mpumulo wako;Pakuti Yehova anakucitira cokoma.

8. Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa,Maso anga kumisozi, Mapazi anga, ndingagwe.

9. Ndidzayenda pamaso pa Yehova M'dziko la amoyo.

10. Ndinakhulupirira, cifukwa cace ndinalankhula;Ndinazunzika kwambiri.

11. Pofulumizidwa mtima ndinati ine,Anthu Onse nga mabodza.

12. Ndidzabwezera Yehova cianiCifukwa ca zokoma zace zonse anandicitira?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 116