8. Adzafanana nao iwo akuwapanga;Ndi onse akuwakhulupirira,
9. Israyeli, khulupirira Yehova:Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.
10. Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova:Ndiye mthandizi wao, ndi cikopa cao.
11. Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova;Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.
12. Yehova watikumbukila; adzatidalitsa:Adzadalitsa nyumba ya Israyeli;Adzadalitsa nyumba ya Aroni.
13. Adzadalitsa iwo akuopa Yehova,Ang'ono ndi akuru.
14. Yehova akuonjezereni dalitso, Inu ndi ana anu.
15. Odalitsika inu a kwa Yehova,Wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16. Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova;Koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.
17. Akufa salemekeza Yehova,Kapena ali yense wakutsikira kuli cete:
18. Koma ife tidzalemekeza YehovaKuyambira tsopano kufikira nthawi yonse.Haleluya.