Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 115:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Manja ali nao, koma osagwira;Mapazi ali nao, koma osayenda;Kapena sanena pammero pao,

8. Adzafanana nao iwo akuwapanga;Ndi onse akuwakhulupirira,

9. Israyeli, khulupirira Yehova:Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.

10. Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova:Ndiye mthandizi wao, ndi cikopa cao.

11. Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova;Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.

12. Yehova watikumbukila; adzatidalitsa:Adzadalitsa nyumba ya Israyeli;Adzadalitsa nyumba ya Aroni.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 115