Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 115:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai, Koma kwa dzina lanu patsani ulemerero,Cifukwa ca cifundo canu, ndi coonadi canu.

2. Aneneranji amitundu,Ali kuti Mulungu wao?

3. Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba;Acita ciri conse cimkonda.

4. Mafano ao ndiwo a siliva ndi golidi,Nchito za manja a anthu.

5. Pakamwa ali napo, koma osalankhula;Maso ali nao, koma osapenya;

6. Makutu ali nao, koma osamva;Mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 115