1. M'mene Israyeli anaturuka ku Aigupto,Nyumba ya Yakobo kwa anthu a cinenedwe cacilendo;
2. Yuda anakhala malo ace oyera, Israyeli ufumu wace.
3. Nyanjayo inaona, nithawa;Yordano anabwerera m'mbuyo.
4. Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo,Timapiri ngati ana a nkhosa.
5. Unathawanji nawe, nyanja iwe?Unabwerereranji m'mbuyo, Yordano iwe?