2. Mbeu yace idzakhala yamphamvu pa dziko lapansi;Mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.
3. M'nyumba mwace mudzakhala akatundu ndi cuma:Ndi cilungamo cace cikhala cikhalire.
4. Kuupika kuturukira oongoka mtima mumdima;Iye ndiye wacisomo; ndi wansoni ndi wolungama.
5. Wodala munthu wakudtira cifundo, nakongoletsa;Adzalimbika nao mlandu wace poweruzidwa.
6. Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse:Wolunguna adzakumbukika ku nthawi yosatha.
7. Sadzaopa mbiri yoipa;Mtima wace ngwokhazikika, wakhulupirira Yehova.
8. Mtima wace ngwocirikizika, sadzacita mantha,Kufikira ataona cofuna iye pa iwo omsautsa.
9. Anagawagawa, anapatsa aumphawi;Cilungamo cace cikhalitsa kosatha;Nyanga yace idzakwezeka ndi ulemu.
10. Woipa adzaziona, nadzapsa mtima;Adzakukuta mano, nadzasungunuka;Cokhumba oipa cidzatayika.