Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 112:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Haleluya.Wodala munthu wakuopa Yehova,Wakukondwera kwambiri ndi malamulo ace,

2. Mbeu yace idzakhala yamphamvu pa dziko lapansi;Mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.

3. M'nyumba mwace mudzakhala akatundu ndi cuma:Ndi cilungamo cace cikhala cikhalire.

4. Kuupika kuturukira oongoka mtima mumdima;Iye ndiye wacisomo; ndi wansoni ndi wolungama.

5. Wodala munthu wakudtira cifundo, nakongoletsa;Adzalimbika nao mlandu wace poweruzidwa.

6. Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse:Wolunguna adzakumbukika ku nthawi yosatha.

7. Sadzaopa mbiri yoipa;Mtima wace ngwokhazikika, wakhulupirira Yehova.

8. Mtima wace ngwocirikizika, sadzacita mantha,Kufikira ataona cofuna iye pa iwo omsautsa.

9. Anagawagawa, anapatsa aumphawi;Cilungamo cace cikhalitsa kosatha;Nyanga yace idzakwezeka ndi ulemu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 112