Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 110:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani pa dzanja lamanja langa,Kufikira nditaika adani anu copondapo mapazi anu.

2. Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kucokera ku Ziyoni;Citani ufumu pakati pa adani anu.

3. Anthu anu adzadzipereka eni ace tsiku la camuna canu:M'moyera mokometsetsa, mobadwira tnatanda kuca,Muli nae mame a ubwana wanu.

4. Yehova walamulira, ndipo sadzasintha,Inu ndinu wansembe kosathaMonga mwa cilongosoko ca Melikizedeke.

5. Yehova pa dzanja lamanja lakoAdzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wace.

6. Adzaweruza mwa amitundu,Adzadzaza dziko ndi mitembo;Adzaphwanya mitu m'maiko ambiri.

7. Adzamwa ku mtsinje wa panjira;Cifukwa cace adzaweramutsa mutu wace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 110