Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 108:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wakhazikika mtima wanga, Mulungu;Ndidzayimba, inde ndidzayimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.

2. Galamukani, cisakasa ndi zeze;Ndidzauka ndekha mamawa.

3. Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova:Ndipo ndidzayimba zakukulemekezani mwa anthu.

4. Pakuti cifundo canu ncacikuru kupitirira kumwamba,Ndi coonadi canu kufikira mitambo.

5. Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu;Ndi ulemerero wanu pamwamba pa dziko lonse lapansi.

6. Kuti okondedwa anu alanditsidwe,Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutibvomereze.

7. Mulungu analankhula m'ciyero cace; ndidzakondwerera:Ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.

8. Gileadi ndi wanga: Manase ndi wanga;Ndi Efraimu ndiye mphamvu ya mutu wanga;Yuda ndiye wolamulira wanga.

9. Moabu ndiye mkhate wanga;Pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga;Ndidzapfuulira Filistiya,

10. Adzandifikitsa ndani m'mudzi wa m'linga?Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

11. Si ndinu Mulungu, amene mwatitayaOsaturuka nao magulu athu?

12. Tithandizeni mumsauko;Pakuti cipulumutso ca munthu ndi cabe.

13. Mwa Mulungu tidzacita molimbika mtima:Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 108