Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka,Nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

10. Iwo akukhala mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,Omangika ndi kuzunzika ndi citsulo;

11. Popeza anapikisana nao mau a Mulungu,Napeputsa uphungu wa Wam'mwambamwamba;

12. Kotero kuti anagonjetsa mtima wao ndi cobvuta;Iwowa anakhumudwa koma panalibe mthandizi.

13. Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao,Ndipo anawapulumutsa m'kupsinjika kwao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107