Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:37-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Nafese m'minda, naoke mipesa,Ndiyo vakubata zipatso zolemeza.

38. Ndipo awadalitsa, kotero kuti, acuruka kwambiri;Osacepsanso zoweta zao.

39. Koma acepanso, nawerama,Cifukwa ca cisautso, coipa ndi cisoni.

40. Atsanulira cimpepulo pa akulu,Nawasokeretsa m'cipululu mopanda njira.

41. Koma aika waumphawi pamsanje posazunzika,Nampatsa mabanja ngati gulu la nkhosa.

42. Oongoka mtima adzaciona nadzasekera;Koma cosalungama conse citseka pakamwa pace.

43. Wokhala nazo nzeru asamalire izi,Ndipo azindikire zacifundo za Yehova,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107