Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:36-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Ndi apo akhalitsa anjala,Kuti amangeko mudzi wokhalamo anthu;

37. Nafese m'minda, naoke mipesa,Ndiyo vakubata zipatso zolemeza.

38. Ndipo awadalitsa, kotero kuti, acuruka kwambiri;Osacepsanso zoweta zao.

39. Koma acepanso, nawerama,Cifukwa ca cisautso, coipa ndi cisoni.

40. Atsanulira cimpepulo pa akulu,Nawasokeretsa m'cipululu mopanda njira.

41. Koma aika waumphawi pamsanje posazunzika,Nampatsa mabanja ngati gulu la nkhosa.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107