30. Pamenepo akondwera, popeza pagwabata;Ndipo Iye awatsogolera kudooko afumko.
31. Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!
32. Amkwezenso mu msonkhano wa anthu,Namlemekeze pokhala akulu.
33. Asanduliza mitsinje ikhale cipululu,Ndi akasupe a madzi akhale nthaka youma;