Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Iwo akutsikira kunyanja nalowa m'zombo,Akucita nchito zao pa madzi akuru;

24. Iwowa apenya nchito za Yehova,Ndi zodabwiza zace m'madzi ozama.

25. Popeza anena, nautsa namondwe,Amene autsa mafunde ace.

26. Akwera kuthambo, atsikira kozama;Mtima wao usungunuka naco coipaco.

27. Adzandira napambanitsa miyendo ngati munthu woledzeta,Nathedwa nzeru konse.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107