Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

22. Ndipo apereke nsembe zaciyamiko,Nafotokozere nchito zace ndi kupfuula mokondwera.

23. Iwo akutsikira kunyanja nalowa m'zombo,Akucita nchito zao pa madzi akuru;

24. Iwowa apenya nchito za Yehova,Ndi zodabwiza zace m'madzi ozama.

25. Popeza anena, nautsa namondwe,Amene autsa mafunde ace.

26. Akwera kuthambo, atsikira kozama;Mtima wao usungunuka naco coipaco.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107