Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Popeza anapikisana nao mau a Mulungu,Napeputsa uphungu wa Wam'mwambamwamba;

12. Kotero kuti anagonjetsa mtima wao ndi cobvuta;Iwowa anakhumudwa koma panalibe mthandizi.

13. Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao,Ndipo anawapulumutsa m'kupsinjika kwao.

14. Anawaturutsa mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,Nadula zomangira zao.

15. Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

16. Popeza adaswa zitseko zamkuwa,Natyola mipiringidzo yacitsulo.

17. Anthu opusa azunzika cifukwa ca zolakwa zao,Ndi cifukwa ca mphulupulu zao.

18. Mtima wao unyansidwa naco cakudya ciri conse;Ndipo ayandikira zipata za imfa.

19. Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao,Ndipo awapulumutsa m'kupsinjika kwao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107