Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino;Pakuti cifundo cace ncosatha.

2. Atere oomboledwa a Yehova,Amene anawaombola m'dzanja la wosautsa;

3. Nawasokolotsa kumaiko,Kucokera kum'mawa ndi kumadzulo,Kumpoto ndi kunyanja.

4. Anasokera m'cipululu, m'njira yopanda anthu;Osapeza mudzi wokhalamo.

5. Anamva njala ndi ludzu,Moyo wao unakomoka m'kati mwao.

6. Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao,Ndipo anawalanditsa m'kupsinjika kwao.

7. Ndipo anawatsogolera pa njira yolunjika,Kuti amuke ku mudzi wokhalamo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107