Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 107:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino;Pakuti cifundo cace ncosatha.

2. Atere oomboledwa a Yehova,Amene anawaombola m'dzanja la wosautsa;

3. Nawasokolotsa kumaiko,Kucokera kum'mawa ndi kumadzulo,Kumpoto ndi kunyanja.

4. Anasokera m'cipululu, m'njira yopanda anthu;Osapeza mudzi wokhalamo.

5. Anamva njala ndi ludzu,Moyo wao unakomoka m'kati mwao.

6. Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao,Ndipo anawalanditsa m'kupsinjika kwao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 107