Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:41-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo anawapereka m'manja a amitundu;Ndipo odana nao anacita ufumu pa iwo.

42. Adani ao anawasautsanso,Nawagonjetsa agwire mwendo wao.

43. Iye anawalanditsa kawiri kawiri;Koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao,Ndi mphulupulu zao zinawafoketsa,

44. Koma anapenya nsautso yao,Pakumva kupfuula kwao:

45. Ndipo anawakumbukila cipangano cace,Naleza monga mwa kucuruka kwa cifundo cace.

46. Ndipo anawacitira kuti apeze nsoniPamaso pa onse amene adawamanga ndende.

47. Tipulumutseni, Yehova, Mulungu wathu,Ndi kutisokolotsa kwa amitundu,Kuti tiyamike dzina lanu loyera,Ndi kudzitamandira naco cilemekezo canu.

48. Wodala Yehova, Mulungu wa Israyeli,Kuyambira kosayamba kufikira kosatha.Ndi anthu onse anene, Amen.Haleluya,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106