Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:40-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Potero udayaka mkwiyo wa Yehova pa anthu ace,Nanyansidwa Iye ndi colowa cace.

41. Ndipo anawapereka m'manja a amitundu;Ndipo odana nao anacita ufumu pa iwo.

42. Adani ao anawasautsanso,Nawagonjetsa agwire mwendo wao.

43. Iye anawalanditsa kawiri kawiri;Koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao,Ndi mphulupulu zao zinawafoketsa,

44. Koma anapenya nsautso yao,Pakumva kupfuula kwao:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106