40. Potero udayaka mkwiyo wa Yehova pa anthu ace,Nanyansidwa Iye ndi colowa cace.
41. Ndipo anawapereka m'manja a amitundu;Ndipo odana nao anacita ufumu pa iwo.
42. Adani ao anawasautsanso,Nawagonjetsa agwire mwendo wao.
43. Iye anawalanditsa kawiri kawiri;Koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao,Ndi mphulupulu zao zinawafoketsa,
44. Koma anapenya nsautso yao,Pakumva kupfuula kwao: