Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Odala iwo amene asunga ciweruzo,Iye amene acita cilungamo nthawi zonse.

4. Mundikumbukile, Yehova, monga momwe mubvomerezana ndi anthu anu;Mundionetsa cipulumutso canu:

5. Kuti ndione cokomaco ca osankhika anu,Kuti ndikondwere naco cikondwerero ca anthu anu,Kuti ndidzitamandire pamodzi ndi colowa canu.

6. Talakwa pamodzi ndi makolo athu;Tacita mphulupulu, tacita coipa.

7. Makolo athu sanadziwitsa zodabwiza zanu m'Aigupto;Sanakumbukila zacifundo zanu zaunyinji;Koma anapikisana ndi Inu kunyanja, ku Nyanja Yofiira.

8. Koma anawapulumutsa cifukwa ca dzina lace,Kuti adziwitse cimphamvu cace.

9. Ndipo anadzudzula Nyanja Yofiira, niiphwa:Potero anawayendetsa mozama ngati m'cipululu.

10. Ndipo anawapulumutsa m'dzanja la iye amene anawada,Nawaombola ku dzanja la mdani.

11. Ndipo madziwo anamiza owasautsa;Sanatsala mmodzi yense.

12. Pamenepo anabvomereza mau ace;Anayimbira comlemekeza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106