Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 106:20-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. M'mwemo anasintha ulemerero waoNdi fanizo la ng'ombe Yakudya msipu.

21. Anaiwala Mulungu mpulumutsi wao,Amene anacita zazikulu m'Aigupto;

22. Zodabwiza m'dziko la Hamu,Zoopsa ku Nyanja Yofiira.

23. Potero Iye adati awaononge,Pakadapanda Mose wosankhika wace, kuima pamaso pace pagamukapo,Kubweza ukali wace ungawaononge,

24. Anapeputsanso dziko lofunika,Osabvomereza mau ace;

25. Koma anadandaula m'mahema mwao,Osamvera mau a Yehova.

26. Potero anawasamulira dzanja lace,Kuti awagwetse m'cipululu:

27. Kugwetsanso mbeu zao mwa amitundu,Ndi kuwabalalitsa m'maiko maiko.

28. Ndipo anadzipatikiza ndi BaalaPeori,Nadyanso nsembe za akufa.

29. Ndipo anamkwiyitsa nazo zocita zao;Kotero kuti mliri unawagwera.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 106